Mkuluwiko | Tanthauzo |
---|---|
Tikonzetikonze adanyula maliro aeni. | Munthu usamajijirika pa zinthu za eni chifukwa ukhoza kupezeka pavuto lina lake utalakwitsa china chake. |
Ulenje umasimba wako. | Munthu uzisimba zokhudza iwe osati zokhudza anthu ena. |
Galu wamkota sakandira pachabe. |
Wamkulu akamanena kapena kuchita zinthu sangochitapo chabe mopanda kudziwa chomwe akunena kapena kuchita. |
Kunena kwa ndithendithe nanthambwe adadzitengera. |
Si bwino kufulumira kuwulula zinsinsi za ena chifukwa kuteroko ukhoza kupalamula nako. |
Tsabola wakale sawawa. |
Zakale zilibe ntchito. |
Mawu aakulu akoma akagonera. | Nzeru za aakulu zimawoneka phindu lake pakapita nthawi. |
Patsala paja pagona chinziri. | Kunena nkhani zakale pofuna kukometsa zinthu pa mlandu. |
Chetechete sawutsa nyama. | Kungokhala chete sikupindula kanthu ngati munthu akufuna kukwaniritsa chimene akufuna. |
Ntchenzi idamva mawu oyamba. |
|
Kulamula vumbwe n'kulinga uli ndi nkhuku. |
|
Tsoka nsinde chimanga chilinda moto. |
|
Ili kutali mvula mpesa umera ng'amba. |
|
Mlendo ndi amene adza n'kalumo kakuthwa. |
|
Mbuto ya kalulu idakula n'tadzawonani. |
|
Makale sapanganika, adalira m'thumba la mbala. |
|
Khoswe wapadenga/patsindwi adawululitsa wapadzala. |
|
Mthanga kunena adapisa likogwe wa apongozi. |
|
Wakufa sadziwika. |
|
Chifundo chidapha msemamitondo. |
|
Nyama yaliwuma idafa ndi ludzu. |
|
Maso aipsa, kamwa likonza. |
|
Nyalugwe chepsa cha mnzake, iye akapha chiwala achita chokoka. |
|
Nyumba ya mwini sawotchera mbewa. |
|
Nguluwe idalira msampha utaning'a. |
|
Ukatchula mkango kwera m'mwamba. |
|
Suzumire adaphetsa mkhalakale. |
|
| |
Lungalunga mpobadwa chilema chichita kudza. |
|
Linda madzi apite ndipo uziti ndadala. |
|
Ndawonera momwemu mwambi wa gulugufe. |
|
Nkhuyu zodya mwana zidapota akulu. |
|
Kumbire adamka nawo kumanda. |
|
Wokoma atani wonga fungwe. |
|
Ndim'khulupirira adam'gonetsa m'nkhufi. |
|
Mwana wa pang'ona salephera kuyangala. |
|
Tsoka sasimba koma mwayi. |
|
Papsa tonola, sudziwa mtima wa moto. |
|
(a) Mamveramvera adachotsa zolo pa ukwati. (b)Wawona nkhanga mawanga wataya nkhwali. |
|
Mako ndi mako usamuwone kuchepa mwendo. |
|
Konza kapansi kuti kam'mwamba katsike. |
|
Choka m'mbuyo khwangwala atole mphutsi. |
|
Pita uko si kuyenda. | Si bwino pamene muli paulendo umodzi kupangana kuti dzera uko chifukwa paulendo wotero kumavuta kukumana kwake. |
Mbalame zomamwera chigobi chimodzi zimadziwana nthenga. | Anthu ochita zofanana amayendera limodzi ndi kudziwana kwambiri zochita zawo. |
(a) Uchembere n'kudyerana. (b) Kachipande katherere kakoma n'kuyenderana. (c) Lende (katungwe) n'kukankhana. (d) Mnzako akakuti konzu, nawe umam'ti konzu (e) Dombolo n'kuwombolana, nthengu adawombola njiwa. | Tanthauzo: Zinthu zimakhala bwino kumathandizana osati māmodzi yekhayekhayo kumathandiza mnzake. |
Mapanga awiri avumbwitsa. | Kuchita zinthu ziwiri nthawi imodzi kumapezetsa mavuto kapena kumalepheretsa zinthu kuti zichitike bwino. |
Taleka n'talawa adatha mphika. | Munthu akaganiza zoyerekeza kuyamba kuchita chinthu, kumakhala kovuta kudziletsa kuchichita chinthucho chifukwa amafika pochizolowera. |
Mnzako akapsa ndevu mzimire mawa adzazima zako. | Mnzathu akakhala pa mavuto tim'thandize popeza mawa lake akhoza kudzatithandiza ife. |
Akuluakulu ndi m'dambo mozimira moto. | Akuluakulu ndiwo amathandiza zinthu zikafika povuta. |
Za kumzinda sawulula. | Ndi bwino kuti tizisunga chinsinsi cha zimene tawona |